WOSEWELA APAMWAMBA ALIPO


A MPINGANJIRA ATSIMIKIZA KUTI TEAM YAWO ILI NDI OSEWELA APAMWAMBA OMWE ANGATHE KUMENYA CAF CHAMPIONS LEAGUE 

Pulezidenti watimu ya Mighty Wanderers, Dr Thomson Mpinganjira wati timuyi ili ndi osewera a pamwamba omwe ali ndikuthekera kochita zakupsa m'mipikisano yosiyanasiyana ya m'dziko muno kuphatikizapo ya kunja monga yokonzedwa ndi CAF.

A Mpinganjira alankhula izi pomwe amatsimikiza kuti timuyi isewera nawo mumpikisano wa CAF Champions League wa chaka chino kufikira chaka cha mawa. 

Wanderers isewera CAF Champions League potsatira kukhala akatswiri a ligi yaikulu ya m'dziko muno ya Supa Ligi.

Chaka chatha team ya Mighty Wanderers FC inatenga nawo gawo mu CAF confederation cup kamba kokhala akatsiri a Mpikisano wa Castel Challenge Cup wa chaka cha 2024.

Wolemba: Steven Pangani 



Comments

Post a Comment

Popular posts from this blog

MWAMBO UWONESEDWA PA KANEMA

ON THE WAY TO WOMEN FIFA U20

IRAN WITHDRAW FIFA WORLD CUP