WABWELERA
KUCHEDWA KWA CHIPHASO CHOYENDELA KWASOKONEZA ZINTHU
Otchinga pagolo wakale wa matimu a Bangwe All Stars, Ekhaya FC komanso FCB Nyasa Big Bullets Reserve, Elias Missi, wabwerera kumudzi kuchokera ku timu ya Dynamos FC yaku Zimbabwe kamba kakuchedwa kutuluka kwa chiphanso chake choyendera.
Missi anapita kutimuyi komwe amachita zokonzekera ndi anzake pogwiritsa ntchito pepala ngati chilolezo cholowera m'dzikoli.
Koma kutatsala pang'ono kuti ligi yaikulu ku Zimbabwe iyambe, akulu-akulu a timuyi anamuuza kuti akatenge chitupa choyendera ndicholinga choti amulembe ntchito.
"Amwene zandivuta kamba koti passport yanga inali isanatuluke. Koma akulu-akulu a timuyi anditsimikizira kuti andiitananso chaka cha mawa.
"Nditsimikize pano kuti nditumikira kunkuno potengera kuti matimu ena ayamba kale kugogoda," watero Missi.
Wolemba: Steven Pangani
Source: TimveniSportsDesk
Kanema: Kuwonesa zochitika Za Elias Misi
Comments
Post a Comment