OSEWELA ALIPO KALE
Timu ya Civil Service United yalengeza kuti sikukhala mwayi woyesa osewera omwe ali ndi khumbo lofuna kutumikira timuyi pomwe akuyamba zokonzekera zawo.
Timuyi yanena izi pomwe yalengeza kuti ikuyamba zokonzekera zawo za ligi ya 2026-27 pa 10 March 2026.
Iwo akuti akhalabe ndi osewera omwe anali nawo mu ligi ya chaka chatha komanso osewera omwe afika kale kutimuyi patsogolo pa ligiyi.
Izi zapangisa kuti wosewela omwe amayembekezela kuyesa mwayi ku timuyi kuti agwidwe njakata. Ndipo ena mwa iwo apitilizabe kuyesa Mwayi Kuma timu ena omwe alowa kumene ku ligi yayikulu ya dziko muno.
Wolemba: Steven Pangani
Kanema: kuwoneka timu ya Civil Service United in Green Jersey
Comments
Post a Comment